Bushiri wakanitsitsa za ndale: “ Chonde sindikuyambisa chipani, sindikupisana nawo, siyani kufalisa izi.”

M’neneri Shepherd Bushiri wati alibe malingaliro ofuna kuyamba ndale kapena kupikisana nawo pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko chaka cha mawa.

A Bushiri, omwe ndi mtsogoleri wa mpingo wa ECG-The Jesus Nation ati iwo ndi mtumiki wa Mulungu amene cholinga chawo chakhazikika pogwira ntchito ndi boma lolamula ndipo adzapitiriza kutero.

Yemwe amawayankhulira, Aubrey Kusakala wati a Bushiri ndi wokhudzidwa ndi zimene anthu maka m’masamba a mchezo akhala akufalitsa kuti adzapikisana nawo pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko.

A Kusakala apempha anthu amene akufalitsa izi kuti asiye kutero.

Pakadalipano, a Bushiri akuzungulira m’maboma a mdziko lino kugawa chimanga kwa anthu omwe akhudzidwa ndi njala yomwe yayala mphasa.

Iwo adati akufuna kufikira anthu okwana 1 million ndi thandizoli.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Usi asks clergy to pray against cyclone politics between Chilima and Chakwera

Vice President of UTM, Dr. Michael Usi, has asked the clergy in the country to pray for the nation that...

Close