Ana sukulu pa Soche Technical achita ziwonesero kamba ati akungodya nyemba basi
Kwavuta ku Soche Technical College ku Blantyre komwe ana a sukulu akutseka misewu kamba kokwiya kuti miyezi ikudusa koma akungolandira zakudya zomwe ndiwo zake ndi nyemba basi.
Wachiwiri wa Student Union Council pa sukulupo a Tiyanjane Chisowire wati ndiwodandaula chifuwa ma sabata akwana anayi tsopano chitsegulire sukuluyi koma ndiwo zimangokhala nyemba basi.
Mtsogoleri wa sukuluyi panopa akuyesesa kuti akambirane ndi ana asukuluwa ndipo chigulu cha a Polisi chafika kale kuzathandizira kubweresa bata.
Follow and Subscribe Nyasa TV :