Chakwera, mavenda achigawo chakumvuma agwirizana zogwira ntchito limodzi potukula Malawi

Mtsogoleri wa dziko la Dr. Lazarus McCarthy Chakwera Lachinayi madzulo adakumana ndi kukambirana ndi ochita malonda ochokera ku chigawo chakumvuma cha dziko pofuna kulimbikitsa ubale ndi umodzi potukula Malawi.

Mkumanowo udachitikira ku nyumba ya boma ya Chikoko Bay State Lodge ndipo udayitanitsidwa ndi cholinga chowapatsa mavendawa mwayi wokumana ndi mtsogoleri wa dziko.

Polankhula pa mkumanowo, Chakwera adati iye akudziwa mavuto omwe ochita malonda akukumana nawo mdziko muno ndipo anatsindika za kudzipereka kwa boma lake kuthana ndi mavutowo.

Mtsogoleriyu anati ochita malonda ali ndi gawo lalikulu kwambiri pa ntchito yotukula dziko lino.

Chakwera anati ichi ndi chifukwa chake boma lakhazikitsa ngongole zosiyanasiyana pofuna kuthandiza amalonda kupeza mpamba wopititsira patsogolo mabizinesi awo.

M’mau awo, mavenda anathokoza mtsogoleriyu kaamba kowapatsa mpata wokumana nawo komanso kumva madandaulo awo.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Chakwera gives hope to Eastern region vendors

It was all smile on Thursday when Malawi President Dr Lazarus McCarthy Chakwera met vendors from the Eastern region. During...

Close