DPP yasosola mipando yambiri ya mankhasala ku Eastern Region

Wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha DPP mchigawo chaku mmawa a Bright Msaka wati ndiokondwa kuti chipanichi chatenga mipando yonse ya m’makhonsolo mchigawochi.

A Msaka ayankhula izi pambuyo pa chisankho cha wapampando wa khonsolo ya boma la Machinga.

 

Khansala Simplex Diwa wasankhidwa kukhala wapampando ndipo wachiwiri wake ndi khansala Davis Weja.

 

A Diwa ati awonetsetsa kuti ndalama za chitukuko zikugwira ntchito yake komanso kuti zitukuko zikutha mu nthawi yake.

 

A Diwa agonjetsa khansala Cidreck Standy wa chipani cha UDF yemwe anali pa mpandowu.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
State wants Mwanamveka, Chiunda joined to Kabambe’s K8.3bn corruption case: Hearing on 6th August

The multi-billion corruption case involving former Reserve Bank of Malawi (RBM) Dr Dalitso Kabambe and his former deputy Henry Mathanga...

Close