Uladi Mussa wapempha nthumwi za MCP kuti ‘chonde, chonde, kavomerezeni Chakwera azayimilenso’

Mkhala kale pa ndale, Uladi Mussa, wapempha nthumwi ku msonkhano waukulu wa chipani cha MCP kuti zikavomereze dzina la mtsogoleri wadziko lino a Lazarus Chakwera kuti adzaimilenso chipanichi pa chisankho cha chaka chamawa.

Polankhula ndi olemba nkhani mumzinda wa Lilongwe, a Mussa ati utsogoleri wa a Chakwera waonetselatu kuti ndi umene ungatulule dziko lino.

 

Malingana ndi a Mussa, kaya wina akayima kupikisana ndi a Chakwera ku convention, ameneyo nthumwi zikamuchititse manyazi povotera a Chakwera.

 

Chipani cha MCP chikuyembekezeka kuchititsa msonkhano wake waukulu kuyambira lachinayi sabata ino.

 

Amene anali wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha DPP mchigawo cha pakati a Zeria Chakale, amene anali omenyera ufulu wa anthu a Redson Munlo, m’busa Mwayi Kamuyambeni, komanso Mayi Agnes Chimbalanga, omwe anali wachiwiri kwa mkulu wa amayi mu DPP, nawonso atsindika kufunika kwakuti chipani cha MCP motsogozedwa ndi a Chakwera apitilire kulamula dziko lino.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Tobacco earning jumps 40% from last year

Figures from AHL Tobacco Sales show that as of last week, shows that Malawi has realised a total of $395.31...

Close